Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Boma lipitiriza kumamvana ndi ma Bishopu a Katolika

M’buyomu: Ma Bishop a mpingo wakatolika ndi mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera.

Boma lati lipitiriza kuyankhulana komanso kumvana ndi ma Bishop a mpingo wa katolika pofuna kupititsa patsogolo miyoyo ya anthu m’dziko muno.

Mneneri wa boma, yemwenso ndi nduna yofalitsa nkhani, a Moses Kunkuyu, anena izi poyankhula ndi MBC potsatira kalata yomwe ma Bishop a Katolika atulutsa lamulungu.

Mu kalatayi, ma Bishopuwa apempha boma kuti lithetse mavuto osiyanasiyana omwe anthu akukumana nawo.

A Kunkuyu, mmau awo, ati boma lipitiriza kuyankhulana ndi ma Bishopuwa pomwenso akutsata njira zoyenera potukula chuma cha dziko lino ndi miyoyo ya anthu.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Kambalazaza condemns suicide

Simeon Boyce

ETHIOPIAN AIRLINES COMMENCES DIRECT FLIGHTS BETWEEN AFRICA AND PAKISTAN

McDonald Chiwayula

Chief Kasumbu re-instated

Sothini Ndazi
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.