Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Boma lipitiriza kumamvana ndi ma Bishopu a Katolika

M’buyomu: Ma Bishop a mpingo wakatolika ndi mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera.

Boma lati lipitiriza kuyankhulana komanso kumvana ndi ma Bishop a mpingo wa katolika pofuna kupititsa patsogolo miyoyo ya anthu m’dziko muno.

Mneneri wa boma, yemwenso ndi nduna yofalitsa nkhani, a Moses Kunkuyu, anena izi poyankhula ndi MBC potsatira kalata yomwe ma Bishop a Katolika atulutsa lamulungu.

Mu kalatayi, ma Bishopuwa apempha boma kuti lithetse mavuto osiyanasiyana omwe anthu akukumana nawo.

A Kunkuyu, mmau awo, ati boma lipitiriza kuyankhulana ndi ma Bishopuwa pomwenso akutsata njira zoyenera potukula chuma cha dziko lino ndi miyoyo ya anthu.

Related posts

SADC calls for removal of all sanctions on Zimbabwe

Rabson Kondowe

Junior staff warned against corruption

MBC Online

Navicha urges chiefs to promote enrolment in CBCCs

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.