Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Local Local News Nkhani

‘Boma ligwirane manja ndi opanga fetereza wa Mbeya’

Kampani ya Nkhokwe Fertilizer Limited yapempha boma kuti liganizire zoyika feteleza wawo pa ndondomeko ya zipangizo zotsika mtengo za AIP chifukwa ali ndi kuthekera kobwezeretsa nthaka m’chimake.

M’modzi mwa akuluakulu a kampaniyi, a Fatima Sanudi, ati ali ndi chikhulupiliro kuti akatswiri amene amapanga fetereza wa Mbeya, amene amamukonza kochokera kuzinyalala, atha kupita patali ndi ntchito zaulimi boma litawathandiza.

Zaka zingapo zapitazo, boma la Malawi linavomereza kugwiritsa ntchito fetereza wa mtunduwu ndipo pakadali pano kampani zambiri m’dziko muno zikumupanga, kuphatikizapo kampani ya Nkhokwe.

Related posts

Mumba pledges volunteers’ labour policies reformation

Romeo Umali

ANNUAL BROADCASTERS CONFERENCE OPENS

MBC Online

Mzuzu tobacco market opens, farmers satisfied with prices

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.