Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Bambo mfumu alimbikitsa anthu kukhala olimbikira pa ntchito za Mulungu

Bambo mfumu Henry Zulu aku St. Patrick Parish ku Area 18 ati malemu Dr Saulos Chilima anali olimbikira pogwira ntchito zampingo komanso kutumikira dziko.

Iwowa anena izi pa mwambo wa misa ya maliro a wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko linoyu.

Pamwambowu panafika akuluakulu osiyanasiyana, kuphatikizapo woimira kampani ya Airtel yomwe Dr Chilima adagwirako ntchito, kudzanso nduna zaboma.

Pali chikonzero kuti tsiku lililonse kudzikhala mwambo wa misa katatu. Mwambo wa Misa wina uchitikanso 12 koloko masana komanso 6 koloko madzulo.

Dr Chilima adamwalira pa ngozi ya ndege yomwe adakwera itagwa mu nkhalango ya Chikangawa.

 

Related posts

Malawi on path to prosperity with AfDB’s support — NAP

Romeo Umali

AFREXIM BANK COMMITS TO GIVE MW $700 MN FOR ECONOMIC RECOVERY

Blessings Kanache

Baba Malondera lauds Chakwera’s administration

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.