Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Atatu amangidwa atatentha munthu

Abambo atatu ali m’chitokosi powaganizira kuti anatentha a Carolyn Suleman, 21, amene akuti anatumiza ndalama zokwana K800,000 kwa munthu osadziwika pa Airtel Money.

Ofalitsankhani pa Polisi ya Lilongwe, a Hastings Chigalu, ati izi zinachitika Lamulungu ku Malangalanga ndipo amene akuwaganizirawa ndi a Doud Yasin, 38, Francis Sadik, 31 ndi Alfred Phiri, 30.

A Chigalu ati a Suleman analandira thenifolo yachilendo m’mawa ndipo anauzidwa kuti apite pa agent aliyense wa Airtel Money kuti atumize ndalamazo kwa anthu atatu ndipo anatumiza ndi a Yasin, amene amachita malonda awo pa sitolo ya Premier Bet ya Mungo.

Atamaliza kutumiza ndalamazo, a Yasin anamufunsa mtsikanayo kuti awapatse koma iye anati alibe komanso anati samamudziwa munthu amene wamuuza kuti atumize ndalamayo.

Bambowa, pamodzi ndi a Sadik komanso a Phiri, amene amagwiranso ntchito ku Premier Bet komweko, anamutengera ochitidwa chipongweyi m’chipinda chosungirako katundu ndi kumuthira petulo wa mu generator ndi kumuyatsa moto.

Kutsatira izi, a Chigalu anati Carolyn anathamangira naye ku chipatala cha Kamuzu Central kumene akulandira thandizo la mankhwala chifukwa wavulala kwambiri thupi lonse.

Atatuwa akuyembekezeka kuyankha mlandu ovulaza munthu.

Related posts

Chakwera to visit flood victims in KK, KA

Romeo Umali

Phungu wa DPP wayamikira boma chifukwa chosakondera

Alinafe Mlamba

New Puma MD determined to make gas cheaper

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.