Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Apolisi kwa Jenda amanga Boma

Apolisi kwa Jenda m’boma la Mzimba amanga a Robert Boma a zaka 34 atawapeza ndi chamba cholemera ma kilo 32 pamene amafuna kuti akwere nacho basi yopita ku Lilongwe.

Ofalitsankhani ku polisi ya Jenda, a MacFarlen Mseteka, akuti akwanitsa kugwira mkuluyu pambuyo potsinidwa khutu kuti a Boma anali ku Luwawa.

Apolisi atathamangirako, a Boma anathawira mu basi yomwe inali pa depoti.

Atawapeza, anawafufuza ndipo anawapeza ndi Chambacho chomwe sanatulutse msonkho wake, ndipo apolisi sanachedwetse koma kuwamanga kuti akayankhe mlandu.

A Boma ndi a m’mudzi wa Chiphazi kwa mfumu yayikulu Kasumbu m’boma la Dedza.

Related posts

Nasser Forum pushes youth integration at 2025 Pan-African Youth Forum

Romeo Umali

POLICE ARREST MUTHARIKA OVER MASS GRAVES

MBC Online

Mafumu asayina mgwirizano wa chitukuko ndi kampani ya Globe Metals and Mining

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.