Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Apolisi kwa Jenda amanga Boma

Apolisi kwa Jenda m’boma la Mzimba amanga a Robert Boma a zaka 34 atawapeza ndi chamba cholemera ma kilo 32 pamene amafuna kuti akwere nacho basi yopita ku Lilongwe.

Ofalitsankhani ku polisi ya Jenda, a MacFarlen Mseteka, akuti akwanitsa kugwira mkuluyu pambuyo potsinidwa khutu kuti a Boma anali ku Luwawa.

Apolisi atathamangirako, a Boma anathawira mu basi yomwe inali pa depoti.

Atawapeza, anawafufuza ndipo anawapeza ndi Chambacho chomwe sanatulutse msonkho wake, ndipo apolisi sanachedwetse koma kuwamanga kuti akayankhe mlandu.

A Boma ndi a m’mudzi wa Chiphazi kwa mfumu yayikulu Kasumbu m’boma la Dedza.

Related posts

BDNC SEALS K10 MN DEAL

MBC Online

Seed company introduces instalments payment for farmers

Romeo Umali

Tiyeni tiphunzirepo pa moyo wa Dr. Chilima – St Patrick’s Parish

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.