Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Apolisi athandiza pantchito yothana ndi mikangano yokhudza malo – Gumba

Nduna yazamalo a Deus Gumba atsindika kufunika kogwira ntchito limodzi ndi apolisi pantchito yolimbana ndi kuthetsa mikangano yokhudza malo m’dziko muno.

Ndunayi yanena izi ku Mponela m’boma la Dowa pa maphunziro ophunzitsa apolisi nkhani yokhudza kukonzedwanso kwa malamulo okhudza malo, komanso ndondomeko zokhudza malo.

A Gumba ati kugwira ntchito limodzi ndi apolisi kuthandiza kuti pasakhale chinyengo komanso mchitidwe olowelera malo, omwe akuti wakula m’dziko muno.

Iwo apemphaso apolisi kuti adziweruza mikangano yokhudza malo mopanda chinyengo.

Komishonala wa apolisi m’chigwawo cha pakati a Emmanuel Soko ati maphunzirowa athandizira kuti apolosi adzigwira ntchito yawo molingana ndi momwe malamulo alili.

 

Olemba : Madalitso Mhango

Related posts

Ligi ipitilira mwezi ukaooneka — Classic U-20 Volleyball

Romeo Umali

SULOM response delayed — Analysts

Romeo Umali

NBM disburses over K5BN loans under ‘Amayi Angathe’ product

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.