Mtsogoleri wa chipani cha Alliance for Democracy (AFORD), a Enoch Chihana, apempha boma kuti pakhale ndondomeko zapadera zothandiza anthu achikulire kuti nawo adzapeze mwayi oponya voti m’zisankho za chaka cha mawa.
Iwo amanena izi pa msonkhano wa ndale omwe chipani chawo chidakonza mu mzinda wa Mzuzu Loweluka masana.
A Chihana ananenetsa zakufunikira kolimbikitsa anthu, kuphatikizapo achikulire, kuti alembetse mu kaundula wa unzika kuti akhale ndi ziphaso ndi cholinga chakuti anthu ochuluka adzakhale ndi mwayi ovota.
Olemba: Musase Cheyo