Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

‘Anthu achikulire akhale ndi mwayi ovota’

Mtsogoleri wa chipani cha Alliance for Democracy (AFORD), a Enoch Chihana, apempha boma kuti pakhale ndondomeko zapadera zothandiza anthu achikulire kuti nawo adzapeze mwayi oponya voti m’zisankho za chaka cha mawa.

Iwo amanena izi pa msonkhano wa ndale omwe chipani chawo chidakonza mu mzinda wa Mzuzu Loweluka masana.

A Chihana ananenetsa zakufunikira kolimbikitsa anthu, kuphatikizapo achikulire, kuti alembetse mu kaundula wa unzika kuti akhale ndi ziphaso ndi cholinga chakuti anthu ochuluka adzakhale ndi mwayi ovota.

Olemba: Musase Cheyo

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Kampani zamigodi ziyike umwini pa MSE — Misalico

Justin Mkweu

Rumphi CSOs push for increased women and youth participation in elections

MBC Online

First Lady to preside over International Women’s Day commemoration

Beatrice Mwape
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.