Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

‘Anthu achikulire akhale ndi mwayi ovota’

Mtsogoleri wa chipani cha Alliance for Democracy (AFORD), a Enoch Chihana, apempha boma kuti pakhale ndondomeko zapadera zothandiza anthu achikulire kuti nawo adzapeze mwayi oponya voti m’zisankho za chaka cha mawa.

Iwo amanena izi pa msonkhano wa ndale omwe chipani chawo chidakonza mu mzinda wa Mzuzu Loweluka masana.

A Chihana ananenetsa zakufunikira kolimbikitsa anthu, kuphatikizapo achikulire, kuti alembetse mu kaundula wa unzika kuti akhale ndi ziphaso ndi cholinga chakuti anthu ochuluka adzakhale ndi mwayi ovota.

Olemba: Musase Cheyo

Related posts

Mavenda ku 25 atseka sitolo ya m’mwenye kaamba kotsitsa mitengo

Mayeso Chikhadzula

UTM yapempha mgwirizano pa nthawi ya maliro

Rabson Kondowe

Moyo Ngwathu boosts education at Mpingu CDSS

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.