Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Andale asamalowelere ntchito zam’ma khonsolo’

Boma lapempha anthu ochita ndale m’dziko muno kuti asamalowelere ntchito za ma khonsolo ndi cholinga chofuna ku kwaniritsa zolinga zawo pa ndale.

Nduna ya za maboma a ang’ono, a Richard Chimwendo Banda, ndi amene ananena izi mu mzinda wa Blantyre pamkumano wa masiku awiri womwe adindo a m’ma khonsolo a m’chigawo cha kumwera amafotokoza momwe agwilira ntchito zawo kwa miyezi ingapo yapitayo.

Ndunayi inapemphanso atsogoleri m’ma khonsolowo kuti azigwira ntchito zotumikira anthu omwe ndi osowa.

A Chimwendo Banda anatinso m’chitidwe wosokoneza ntchito za chitukuko m’ma khonsolo umakula maka pamene dziko likuyandikira kuchita chisankho.

“Musalole kuti ntchito zachitukuko ziime chifukwa chofuna kusangalatsa anthu ena a ndale, ” a Chimwendo Banda anatero.

Pamkumanowu, kunali a bwanankubwa, oyang’anira ntchito za chuma m’ma khonsolo, aphungu akunyumba yamalamulo komanso ma khansala a m’chigawo cha kum’mwera mwa ena.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

M’busa wapereka mimba kwa mtsikana atamunamiza kuti amuchiritsa matenda

Charles Pensulo

‘Kupapira bibida mwachisawawa kukusokoneza chitukuko’

Emmanuel Chikonso

BWALO LA MILANDU LABWEZA GALIMOTO YA UMBONI WABOMA

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.