Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Ali m’chitokosi pobaya ofisala wapolisi

Apolisi m’boma la Mangochi amanga a Arnold Moyowatha, 54, powaganizira kuti anabaya pamimba wapolisi pamene amafuna kuti awamange.

Ofalitsa nkhani za apolisi m’bomali, a Amina Tepani Daudi, ati izi zinachitika pamene apolisi anali pa ntchito yawo yoyendera m’madera amene kumachitika umbanda ndipo a Moyowatha anali ndi anzawo ena awiri amene anathawa.

A Daudi ati pamene a Moyowatha amafuna kuti adzipulumutse anatulutsa mpeni ndi kuvulaza wapolisiyo amene anathamangira naye kuchipatala ndipo anakalandira thandizo.

A Moyowatha ali m’chitokosi pamene akudikira kukaonekera kubwalo la milandu.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

2nd Global Environment Facility (GEF) on Sustainable Forest Management Begins

Kumbukani Phiri

Parliament happy with progress on Likoma jetty construction

MBC Online

Maize restocking exercise on track – ADMARC

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.