Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Alexander ‘Cage’ Likande wamwalira

Katswiri wa nkhonya m’dziko muno, Alexander ‘Cage’ Likande, wamwalira m’bandakucha wa lero pangozi ya njinga yamoto yomwe inaombana ndi galimoto.

Malinga ndi zimene akunena mnzake Byson Gwayani, Likande anachita ngoziyi dzulo usiku akuchokera ku Area 36 mu mzinda wa Lilongwe kumene kunali masewero a nkhonya.

Malipoti akuti atathamangira naye ku chipatala cha Kamuzu Central kuti akalandire thandizo, iye anamwalira.

Mwambo wa maliro a Likande akhale akuwulengeza ndi a kubanja komanso adindo a bungwe loyendetsa nkhonya m’dziko muno la MPBCB.

 

Related posts

40 years in jail for defiling daughter

Romeo Umali

Chakwera assures IMF, World Bank of continued sound economic policies

Mayeso Chikhadzula

Malawi makes strides on access to justice for women, girls

Doreen Sonani
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.