Malawi Broadcasting Corporation
Africa Culture Local News Nkhani

ADABWA NDI KUDABWA KWA MAFUMU

Bungwe la Mulakho wa a Lhomwe lati ndi lodabwa ndi mafumu ena omwe sakumvetsa zakusankha kwa mfumu yatsopano ya a Lhomwe Paramount Chief Kaduya.

Wapampando wa bungwe-li, a Muchanakwaye Mpuluka alankhula izi pamene mafumu ena atatu anauza olembankhani lachisanu lapitali kuti sakugwirizana ndi m’mene asankhila mfumu yatsopanoyi.

Mwambo wa Mlakho wa aLhomwe

Koma a Mpuluka ati anthu-wa anali nawo pazokambirana ndipo onse anagwirizana zosankha a Kaduya ngati mfumu yawo.

Iwo adaonjezeranso kumema ma membala a bungwe lawo kuti apewe kumvera anthu andale amene akufuna kuwagawanitsa.

Lachitatu lapitali, mtsogoleli wa dziko lino Dr. Lazarus Chakwera adavomereza dzina la a Kaduya kuti ikhale mfumu.

Kusankha-ku kunali kukhazikitsa mfumu patadutsa zaka zoposa zisanu, potsatira imfa ya mfumu yaikulu Ngolongoliwa.

Olemba: Blessings Kanache

Related posts

Chakwera akhala nawo pa Misa ya mayi Shanil Dzimbiri

MBC Online

Dzinkambani’s Ntcheu Warriors suffer third consecutive defeat

MBC Online

Ochita malonda apempha ngongole kwa President Chakwera

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.