Malawi Broadcasting Corporation
Culture Local Local News Nkhani

Achewa athira nsembe

Anthu a chikhalidwe cha a Chewa athira nsembe ku Nsinja m’boma la Lilongwe ndipo apempha mphambe kuti akwaniritse zosowa zawo.

Kumwambowu, umene unalipo Loweruka, kunali anthu ochuluka amitundu yosiyanasiyana ya m’dziko muno komanso akuluakulu ochokera ku unduna wa zokopa alendo, unduna waza chikhalidwe ndi amene amayendetsa bungwe la Chewa Heritage Foundation, amene amatsogolera mwambowu.

Mwambowu ndi umodzi mwa miyambo ya a Chewa umene umachitika chaka ndi chaka ndipo umathandiza kubweretsa umodzi ndi mtendere pakati pa anthu amitundu yosiyana amene amakumana pa mwambowu.

Olemba: Ida Chiwaya

Related posts

Wildlife crime surge worries Nkhotakota Wildlife Reserve

Rabson Kondowe

PRSM to host high-level interface on trust and reputation in development agenda

McDonald Chiwayula

Nsanje DC pushes for irrigation farming

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.