Malawi Broadcasting Corporation
Culture Local Local News Nkhani

Achewa athira nsembe

Anthu a chikhalidwe cha a Chewa athira nsembe ku Nsinja m’boma la Lilongwe ndipo apempha mphambe kuti akwaniritse zosowa zawo.

Kumwambowu, umene unalipo Loweruka, kunali anthu ochuluka amitundu yosiyanasiyana ya m’dziko muno komanso akuluakulu ochokera ku unduna wa zokopa alendo, unduna waza chikhalidwe ndi amene amayendetsa bungwe la Chewa Heritage Foundation, amene amatsogolera mwambowu.

Mwambowu ndi umodzi mwa miyambo ya a Chewa umene umachitika chaka ndi chaka ndipo umathandiza kubweretsa umodzi ndi mtendere pakati pa anthu amitundu yosiyana amene amakumana pa mwambowu.

Olemba: Ida Chiwaya

Related posts

Msukwa elected Chairperson of KA District Council

Alinafe Mlamba

Residents concerned over waste accumulation at Karonga Main Market

MBC Online

Anglican Church offers free secondary education in BT

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.