Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani

A Kasambara awayika m’manda pa mwambo wachisilikali

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera walamula kuti malemu a Raphael Kasambara ayikidwe m’manda potsatira mwambo wachisilikali.

Pakalinpano mwambo oika m’manda malemuwa uli mkati m’mudzi mwa Chijere m’boma la Nkhata Bay.

A Kasambara anali katswiri pa nkhani za malamulo ndipo anamwalira pa 7 June 2024 mu mzinda wa Lilongwe. Iwo anakhalaponso nduna yoona za malamulo komanso mkulu oyimira boma pa milandu (Attorney General) ndipo anabadwa m’chaka cha 1969.

 

Related posts

Chilemba waona nyenyezi ku Russia

Rabson Kondowe

THE DREAD OF THE GOLDEN YEARS

McDonald Chiwayula

KAMPANI ZACHITA BWINO CHAKA CHATHA— MCCCI

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.