Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

A Kabambe achoka atakhumudwa — Mwakasungula

Oyankhulapo pa nkhani za ndale a Undule Mwakasungula ati kuchoka kwa a Dalitso Kabambe ku chipani Democratic Progressive (DPP) kutha kukhala kukhumudwa chifukwa a Peter Mutharika, mtsogoleri wa chipanichi, m’mbuyomu adanenetsa kuti ayimira ngati mtsogoleri pa zisankho za chaka cha mawa.

A Kabambe m’mbuyomu akhala akuonetsa chidwi chofuna kudzayimira ngati mtsogoleri wa DPP.

A Mwakasungula alangiza a Kabambe, amene alengeza lero kuti achoka mu chipani cha DPP, kuti abwere poyera ndikufotokoza za kumene alowere komanso zimene achite.

Masana a Lolemba, a Kabambe, kudzera mu chikalata, anati iwo a choka m’chipanichi ataganizira mozama komanso anadziwitsa m’tsogoleri wa chipanichi, a Mutharika.

Kalata ya a Kabambe

Ofalitsa nkhani ku DPP, a Shadric Namalomba, anakana kuyankhulapo pa nkhaniyi.

A Kabambe adagwirapo ntchito ngati gavanala wa Reserve Bank of Malawi.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mwanyali wins Mzuzu Half Marathon again

MBC Online

‘Respect the rights of people with disabilities’

Sothini Ndazi

POLICE APPREHEND HEALTH WORKER OVER ALLEGED RAPE

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.