Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

A Kabambe achoka atakhumudwa — Mwakasungula

Oyankhulapo pa nkhani za ndale a Undule Mwakasungula ati kuchoka kwa a Dalitso Kabambe ku chipani Democratic Progressive (DPP) kutha kukhala kukhumudwa chifukwa a Peter Mutharika, mtsogoleri wa chipanichi, m’mbuyomu adanenetsa kuti ayimira ngati mtsogoleri pa zisankho za chaka cha mawa.

A Kabambe m’mbuyomu akhala akuonetsa chidwi chofuna kudzayimira ngati mtsogoleri wa DPP.

A Mwakasungula alangiza a Kabambe, amene alengeza lero kuti achoka mu chipani cha DPP, kuti abwere poyera ndikufotokoza za kumene alowere komanso zimene achite.

Masana a Lolemba, a Kabambe, kudzera mu chikalata, anati iwo a choka m’chipanichi ataganizira mozama komanso anadziwitsa m’tsogoleri wa chipanichi, a Mutharika.

Kalata ya a Kabambe

Ofalitsa nkhani ku DPP, a Shadric Namalomba, anakana kuyankhulapo pa nkhaniyi.

A Kabambe adagwirapo ntchito ngati gavanala wa Reserve Bank of Malawi.

 

Related posts

SUSU IN MALAWI

Mayeso Chikhadzula

Ombudsman orders Lands Ministry to release backlog of land applications

Rabson Kondowe

Malawi hockey team heads to Zambia for Zambezi Test Series

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.