Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

A Kabambe achoka atakhumudwa — Mwakasungula

Oyankhulapo pa nkhani za ndale a Undule Mwakasungula ati kuchoka kwa a Dalitso Kabambe ku chipani Democratic Progressive (DPP) kutha kukhala kukhumudwa chifukwa a Peter Mutharika, mtsogoleri wa chipanichi, m’mbuyomu adanenetsa kuti ayimira ngati mtsogoleri pa zisankho za chaka cha mawa.

A Kabambe m’mbuyomu akhala akuonetsa chidwi chofuna kudzayimira ngati mtsogoleri wa DPP.

A Mwakasungula alangiza a Kabambe, amene alengeza lero kuti achoka mu chipani cha DPP, kuti abwere poyera ndikufotokoza za kumene alowere komanso zimene achite.

Masana a Lolemba, a Kabambe, kudzera mu chikalata, anati iwo a choka m’chipanichi ataganizira mozama komanso anadziwitsa m’tsogoleri wa chipanichi, a Mutharika.

Kalata ya a Kabambe

Ofalitsa nkhani ku DPP, a Shadric Namalomba, anakana kuyankhulapo pa nkhaniyi.

A Kabambe adagwirapo ntchito ngati gavanala wa Reserve Bank of Malawi.

 

Related posts

Chitipa road accident claim life

Romeo Umali

New solar initiative to boost MSMEs and drive economic growth

McDonald Chiwayula

Thin plastic saga takes new twist

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.