Malawi Broadcasting Corporation
International

Mulungu adalitse Iran komanso Israel — Trump

Mtsogoleri wa dziko la America, a Donald Trump, ayamikira mayiko a Israel ndi Iran kaamba koonetsa chidwi chothetsa nkhondo, malinga ndi nyumba youlutsa mawu ya BBC.

Izi zilichomwechi pamene dziko la Iran linaponya mizinga kumalo a asilikali a America m’dziko la Qatar ngati kubwezera zimene dziko la America ndi Israel anachita posakaza malo a nuclear ku Iran.

Pakadalipano, Israel yavomera kuleka kumenya nkhondo ndi Iran.

M’mawu ake, nduna yoona nkhani za kunja kwa dziko la Iran, a Seyed Araghchi, ati dziko lawo lichita chimodzimodzi ngati Israel itasiya kuchitira chiwembu dziko lawo.

Olemba: Telson Magombo

Related posts

Chakwera attending memorial service for late Namibian President Hage Geingob

Rabson Kondowe

Moroccan Envoy hails King Mohammed VI’s vision on Sahara

McDonald Chiwayula

AFRICA’S INTENSIFYING HEATWAVES SHOW URGENT NEED FOR FINANCE

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.