Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

COSOMA ipereka ndalama kwa oyimba

Bungwe la oyimba la Copy right Society of Malawi (COSOMA) lati mawa lipereka ndalama za nkhaninkhani kwa oyimba m’dziko muno kudzera ku thumba la bungwe la Malawi Revenue Authority la  Blank Media Levy.

Wapampando wa bodi ya COSOMA, Reverend Chimwemwe Mhango, watsimikiza izi.

“Pali oyimba ambiri amene mawa lino alandira ma million kuposa momwe tinapelekera m’mbuyomu koma nditsindike kuti ndalamazi sitipereka kwa oyimba wina aliyense amene ndi membala wa bungwe la COSOMA koma tipereka kwa oyimba okhawo amene nyimbo zawo anthu akhala akuzigawana pogwiritsa zipangizo za digital monga lamya za m’manja, pa kompyuta komanso pa internet kudzera pa masamba a mchezo,” atero a Mhango.

M’mbuyomu kwakhala kuli maphokoso pa ndondomeko yomwe bungwe la COSOMA limatsata posankha oyimba amene alandire ndalamazi.

Mwambowu uchitikira munzinda wa Lilongwe.

Related posts

Major Flora Selemani-Ngwilinji’s inspirational story

Rabson Kondowe

Wanderers leapfrog to 4th place

Romeo Umali

POLICE PLEDGE TIGHT SECURITY IN LIMBE

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.