Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local Local News Nkhani

MAIIC yapanga phindu lokwana K2.5 billion mu 2023

Bungwe la Malawi Agriculture and Industrial Investment Corporation (MAIIC) lapanga phindu lokwana K2.5 billion chaka chatha poyerekeza ndi K722 million mu chaka cha 2022, malinga ndi kalata yazachuma yomwe bungweli lasindikiza.

Bungweli linakhazikitsidwa ndicholinga chobwereketsa ndalama kwa alimi komanso ena amene akupanga zamafakitale.

Mkulu wogwirizira wabungweli, a Lloyd Banda, ati phinduli lakwera kamba koti abwereketsa ndalama zambiri m’chakachi.

Iwo ati chinsinsi chawo ndichoti amawunika bwino munthu kapena kampani paza kuthekera kwawo kobweza ngongole.

A Banda anawonjezera kuti m’mene ayambira chaka chino, zikuonetsa kuti apanganso phindu loposa chaka chatha.

 

Related posts

‘Lolemba ndi tchuthi’

Rabson Kondowe

FEDOMA talks inclusion in natural disaster management

Romeo Umali

2025 TNM Super League is another three-horse race — Nyirenda

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.