Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Malaulo: Anjatidwa atagwililira mwana omupeza pofuna kukhwima

Khoti lina m’boma la Phalombe lalamula a Paul Mwina a zaka 35 zakubadwa kuti akagwire jele kwa zaka 14 chifukwa adagwililira mwana omupeza wazaka 12 pofuna kulemera.

Ofalitsankhani pa Polisi ya m’bomali, a Jimmy Kapanja, ati bamboyu adapita kwa sing’anga wina pofuna kukhwima kuti alemere ndipo atabwera ndilufotokozera mkazi wake zoyenera kuchita, sadazengereze koma kulolera malodzawo.

Komabe mwanayo adakatsina khutu m’bale wake, yemwe adakatula nkhaniyi ku Polisi.

A Mwina ndi a m’mudzi mwa Volupo, mfumu yayikulu Nkhulambe m’boma la Phalombe lomwelo.

 

Related posts

Moyo Ngwathu boosts education at Mpingu CDSS

Romeo Umali

Masewero a Darts m’chigawo chapakati apeza thandizo

Romeo Umali

Minister condemns vandalism of school property

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.