Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Malaulo: Anjatidwa atagwililira mwana omupeza pofuna kukhwima

Khoti lina m’boma la Phalombe lalamula a Paul Mwina a zaka 35 zakubadwa kuti akagwire jele kwa zaka 14 chifukwa adagwililira mwana omupeza wazaka 12 pofuna kulemera.

Ofalitsankhani pa Polisi ya m’bomali, a Jimmy Kapanja, ati bamboyu adapita kwa sing’anga wina pofuna kukhwima kuti alemere ndipo atabwera ndilufotokozera mkazi wake zoyenera kuchita, sadazengereze koma kulolera malodzawo.

Komabe mwanayo adakatsina khutu m’bale wake, yemwe adakatula nkhaniyi ku Polisi.

A Mwina ndi a m’mudzi mwa Volupo, mfumu yayikulu Nkhulambe m’boma la Phalombe lomwelo.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Malawi records 1,700 suicide-related deaths

Olive Phiri

MRA donates K60 million to support Cyclone Jude survivors

McDonald Chiwayula

Lero tapereka holo-yi ndipo pompano tiyamba kumanga chipatala – Troughton

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.