Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Malaulo: Anjatidwa atagwililira mwana omupeza pofuna kukhwima

Khoti lina m’boma la Phalombe lalamula a Paul Mwina a zaka 35 zakubadwa kuti akagwire jele kwa zaka 14 chifukwa adagwililira mwana omupeza wazaka 12 pofuna kulemera.

Ofalitsankhani pa Polisi ya m’bomali, a Jimmy Kapanja, ati bamboyu adapita kwa sing’anga wina pofuna kukhwima kuti alemere ndipo atabwera ndilufotokozera mkazi wake zoyenera kuchita, sadazengereze koma kulolera malodzawo.

Komabe mwanayo adakatsina khutu m’bale wake, yemwe adakatula nkhaniyi ku Polisi.

A Mwina ndi a m’mudzi mwa Volupo, mfumu yayikulu Nkhulambe m’boma la Phalombe lomwelo.

 

Related posts

Habitat for Humanity brings hope to Cyclone Freddy survivors

Romeo Umali

CFTC warns against sale, consumption of Cool Drop bottled water batch

Rabson Kondowe

First Lady urges new NAM leadership to unearth talent

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.