Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

‘Timanga wina aliyense oyambitsa ziwawa zandale’

Mkulu wa apolisi m’dziko muno, a Merlyne Yolamu, wachenjeza kuti apolisi athana ndi wina aliyense oyambitsa ziwawa panthawi imene zokonzekera zachisankho zili mkati.

A Yolamu apereka chenjezoli pa msonkhano opereka uthenga olimbana ndi nkhanza zosiyanasiyana, omwe unachitikira m’boma la Mzimba pa Jenda.

“Ndichenjeze pano kuti timanga wina aliyense oyambitsa zisokonezo nthawi ino, lolani wina aliyense apange msonkhano wake mwaufulu posazulirana mbendera kapena kemenyana,” anatero a Yolamu.

Iwo anati a Malawi ndi amodzi ngakhale amasiyana zipani kotero anthu sakuyenera kusankhana.

Olemba: Henry Haukeya

Related posts

Late Hope Chisanu’s funeral service underway in LL

Romeo Umali

Twists and turns on Malawi Stock Exchange (MSE)

Romeo Umali

Sitalaka ya madalaivala yaonongetsa mkaka wa K120 million

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.