Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

The Harps ikondwerera zaka khumi zamaimbidwe ndi makwaya aku Zimbabwe ndi Zambia

Gulu loimba mingoli yauzimu m’dziko muno la The Harps laitana makwaya aku Zambia ndi Zimbabwe pachikondwerero cha zaka khumi zamaimbidwe pomwenso likukhazikitsa chimbale chatsopano.

Makwaya awiriwa ndi Redeemed Family yaku Zimbabwe ndi Sovereign Family yaku Zambia omwe afika m’dziko muno kudzera pabwalo la ndege la Kamuzu ku Lilongwe.

Malinga ndi Owen Nkoka, wapampando wagulu la The Harp, mwambowu uchitika la Mulungu pa BICC mnzinda wa Lilongwe ndipo anthu ayembekezere kutsitsimuka ndi kuona maimbidwe apamwamba.

Wapampando wagulu laku Zimbabwe wati kupatula kuthandiza gulu la m’dziko munoli kwayayi ikuyembekezeka kuimbanso ndi oimba nyimbo zauzimu akuno ku Malawi.

 

Olemba: Emmanuel Chikonso

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

CHILIMA FOR WELL-TRAINED CHAPLAINS

Mayeso Chikhadzula

A Malawi First sachitanso zionetsero zotsutsana ndi chizindikiro cha tax stamp

McDonald Chiwayula

Malawi’s Attorney General joins Commonwealth ministers to champion digital access to justice for 2.5 billion citizens

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.