Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

The Harps ikondwerera zaka khumi zamaimbidwe ndi makwaya aku Zimbabwe ndi Zambia

Gulu loimba mingoli yauzimu m’dziko muno la The Harps laitana makwaya aku Zambia ndi Zimbabwe pachikondwerero cha zaka khumi zamaimbidwe pomwenso likukhazikitsa chimbale chatsopano.

Makwaya awiriwa ndi Redeemed Family yaku Zimbabwe ndi Sovereign Family yaku Zambia omwe afika m’dziko muno kudzera pabwalo la ndege la Kamuzu ku Lilongwe.

Malinga ndi Owen Nkoka, wapampando wagulu la The Harp, mwambowu uchitika la Mulungu pa BICC mnzinda wa Lilongwe ndipo anthu ayembekezere kutsitsimuka ndi kuona maimbidwe apamwamba.

Wapampando wagulu laku Zimbabwe wati kupatula kuthandiza gulu la m’dziko munoli kwayayi ikuyembekezeka kuimbanso ndi oimba nyimbo zauzimu akuno ku Malawi.

 

Olemba: Emmanuel Chikonso

Related posts

Matupi ena angozi ya ndege awaika m’manda masanawa

Romeo Umali

Court bars Kamangila from posting about Judge Manda on social media

Rabson Kondowe

Tsogolo la mlandu wa a Mbedza lioneka masana ano

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.