Malawi Broadcasting Corporation
Education Entertainment Entertainment Local Local News Nkhani

‘Kanema wa Belinda alimbikitsa atsikana’

Amene anajambula kanema wa Belinda, gulu la Remnant Lions, ati ali ndi chikhulupiliro kuti kanemayu alimbikitsa atsikana kuti asamafooke pa maphunziro ngakhale atakumana ndi mavuto, kuphatikizapo kutenga pakati.

Otsogolera ntchito yojambula m’kanemayu, a Tionge Chisiza, ati aonetsetsa kuti seweroli lifikire aliyense, makamaka m’sukulu zakumudzi.

Iwo amayankhula izi Lachisanu madzulo atawonetsa kanemayu mu nzinda wa Lilongwe.

“Tikufuna aliyense yemwe ali ndi chidwi cholimbikitsa maphunziro aonere kanemayi,” a Chisiza anatero.

Kanemayu anamuonetsa kale munzinda wa Blantyre ndipo pali chikonzero kuti akamuonetsenso ku Mzuzu ndi ma boma ena.

Gulu la Remnant Lions analitsogolerako ndi malemu a Thlupego Chisiza.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

ActionAid, CAVWOC launch lean season cash transfer programme

Chisomo Break

Chakwera calls for multisectoral approach to combat lead poisoning in children

Mayeso Chikhadzula

Standard Bank gives K25 million towards 2024 Mother’s Fun Run

Kumbukani Phiri
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.