Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Dr Chakwera achita zokambilana zobweretsa sitima zapamadzi

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera akuyembekezeka kukambirana ndi kampani zoona za sitima zapamadzi ku Germany kuti athandize kuyambitsa ntchito za maulendo pa nyanja ya Malawi pothana ndi mavuto amayendedwe panyanjayi.

Nduna yoona nkhani zakunja a Nancy Tembo anena izi pomwe Dr Chakwera akuyembekezeka kufika ku Frankfurt ku Germany lachitatu kuchokera ku Italy komwe akakambilane ndi makampaniwa.

Iwo ati ali ku Germany, Dr Chakwera akambirana ndi kampaniyi za maulendowa poonjezela kukambirana zankhani ya magetsi asanakumane ndi mtsogoleri wa dziko la Germany.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

President Chakwera apitiliza ulendo m’chigawi cha ku m’mawa

MBC Online

Namondwe Filipo alibe chiopsezo ku Malawi, atero azanyengo

Romeo Umali

‘Malamulo a chipani akuvomereza atosgoleri ake kudzachita mgwirizano ndizipani zina’

Yamikani Simutowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.