Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Chitukuko chisaononge chilengedwe

Nduna yoona zamalo, a Deus Gumba, apempha anthu omwe amagwira ntchito yoyeza malo mdziko muno kuti atenge udindo oteteza zachilengedwe akamagwira ntchito zawo.

Ndunayi yanena izi ku Mangochi komwe yatsegulira msonkhano wapachaka wa masiku atatu wa anthu omwe anazama pazoyeza malo pansi pabungwe la Malawi Institute of Surveyors (MIS) komwe atsindika kuti anthuwa ali ndi udindo owonesetsa kuti zachilengedwe zikutetezeka mdziko muno.

“Chitukuko ndichabwino koma timaona kuti zitukuko zambili zimaononga chilengedwe kotelo anthuwa ali ndi udindo kuti akamavomeleza malo okuti pakhale zitukuko aonesetse kuti chilengedwe chisaonongeke,” anatero a Gumba.

President wabungweri Desmond Namangale wayamika boma chifukwa chowaika anthuwa patsogolo pokonza ma bilo atatu azamalo omwe nyumba ya Malamulo yawavomeleza.

Olemba: Davie Umar
#MBCDigital
#Manthu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Boma lipitiriza kufikitsa zitukuko mmadera onse — Chimwendo Banda

Mayeso Chikhadzula

MEC ionjezera masiku m’gawo loyamba la kalembera

Austin Fukula

Titangwanike pomanga dziko lino – Chakwera

Beatrice Mwape
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.