Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Apolisi amanga anthu 696

Apolisi amanga anthu okwana 696 omwe akuwaganizira kuti apalamula milandu yosiyanasiyana mdziko muno.

Malinga ndi mneneri wa  apolisi mdziko muno a Peter Kalaya, ntchitoyi aigwira masiku atatu kuyambira lachitatu sabata yatha.

A Kalaya atinso apeza katundu osiyanasiyana yemwe akumuganizira kuti ndiobedwa.

Katunduyu ndi monga galimoto ziwiri, zipangizo za magalimoto, mankhwala a mchipatala kudzanso zakudya zosavomerezeka ndi zina zambiri.

Malinga ndi a Kalaya, ntchitoyi yomwe aigwira ndi maiko monga Zimbabwe, South Africa, Zambia, Angola ndi ena,  zithandiza kulimbikitsa maubale a kagwiridwe ka ntchito kabwino kudzanso kukhwimitsa chitetezo mu Africa.

 

Olemba : Ghwabupi Mwabungulu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Alimi aku Lilongwe asonkhanitsa K1.7 biliyoni yochitira ulimi

Emmanuel Chikonso

‘Boma likukumana ndi zovuta polimbana ndi mchitidwe wa nkhanza kwa anthu achikulire’

Beatrice Mwape

Mbali ina ya msewu wa Chiwembe sanamange bwino — Chimwendo Banda

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.