Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Tipitiriza kuthandiza – NBS Bank

Bank ya NBS yathandiza anthu okalamba komanso a ulumali ndi matumba a ufa wa chimanga kummwera kwa boma la Chiradzulu.

Poyankhula popereka thandizoli, mkulu wa Branch ya Limbe, a Twaibu Nnani, ati bankiyi ipitiriza kuthandiza osowa kudzera mu njira zosiyanasiyana.

Ndipo mfumu yaikulu Mpunga yapempha mabungwe akufuna kwabwino kuti athandize mabanja omwe akhudzidwa ndi njala.

Malinga ndi a Mpunga thandizoli ati ndi lapafupifupi K3.5 million.

Wolemba: Blessings Cheleuka

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mafumu ku Mzimba apepesa Dr Chakwera

Beatrice Mwape

UK yathandiza Lake of Stars ndi K169 Miliyoni

Emmanuel Chikonso

Boma likhazikitsa mtukula pakhomo wa m’mizinda mawa

Justin Mkweu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.