Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Chikondwelero chasefukira kwa anthu aku Mapuyu South pakukhazikitsidwa kwa ntchito ya msewu

Kuli chisangalalo chokhachokha mmudzi mwa Mzonde komwe mtsogoleri wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera, akukhazikitsa ntchito yomanga misewu, pansi pantchito ya Millennium Challenge Account.

Anthu ochuluka afika pa bwalo la Mzonde pomwe aikapo kanema yayikulu kuti akhoza kutsatira mwambo onse.

A Lettina Kalumbi a mmudzi mwa Tsabango ndi m’modzi mwa anthu mazanamazana omwe afika kudzaonelera kutsekulira kwa ntchitoyi ndipo akuti iwo ndi anzawo ochuluka ayenda makilomita oposa 5 kuchokera kwa Msundwe kudzaona kukhazikitsidwa kwa ntchitoyi, ati kuti akhale ndi umboni kuti yayambadi.

A Kalumbi akuti ndionyadira poti msewu umenewu ndiofunika pokagulitsa mbewu zawo, yomwe ndi ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Two brothers nabbed over possessing Cannabis without permit

Romeo Umali

Zomba prepared for disasters — DPD

MBC Online

Ndondomeko ya mphamvu ku anthu yachiwiri akuikhazikitsa ku Lilongwe

Austin Fukula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.