Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Chikondwelero chasefukira kwa anthu aku Mapuyu South pakukhazikitsidwa kwa ntchito ya msewu

Kuli chisangalalo chokhachokha mmudzi mwa Mzonde komwe mtsogoleri wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera, akukhazikitsa ntchito yomanga misewu, pansi pantchito ya Millennium Challenge Account.

Anthu ochuluka afika pa bwalo la Mzonde pomwe aikapo kanema yayikulu kuti akhoza kutsatira mwambo onse.

A Lettina Kalumbi a mmudzi mwa Tsabango ndi m’modzi mwa anthu mazanamazana omwe afika kudzaonelera kutsekulira kwa ntchitoyi ndipo akuti iwo ndi anzawo ochuluka ayenda makilomita oposa 5 kuchokera kwa Msundwe kudzaona kukhazikitsidwa kwa ntchitoyi, ati kuti akhale ndi umboni kuti yayambadi.

A Kalumbi akuti ndionyadira poti msewu umenewu ndiofunika pokagulitsa mbewu zawo, yomwe ndi ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku.

Related posts

Apha makwacha ndi ulimi wamakono wa mpunga

Alinafe Mlamba

‘Ntchito yomanga misewu ikuyenda bwino ku Lilongwe’

Mayeso Chikhadzula

MBC ikuchita bwino — Chiyamwaka

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.