Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Chakwera akutsegulira ntchito ya Millennium Challenge Corporation yokonza misewu

Anthu ochuluka akhamukira pabwalo la Mzonde kwa mfumu yaikulu Kalolo ku Lilongwe komwe mtsogoleri wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera, pamodzi ndi mkulu  wa Millennium Challenge Corporation, Madam Alice Albright, akhazikitse ntchito yokonza misewu pansi pa Millennium Challenge Account – Malawi II (MCA-M).

Wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Dr Saulos Chilima, nawonso alinawo kumwambowu.

Malinga ndi mkulu yemwe akutsogolera ntchitoyi kuno ku Malawi, a Dye Mawindo, akangotsekulira zonse zochitika ziyambika.

Ntchitoyi, yomwe ndi ya ndalama zokwana $300 million, ayigwira kwa zaka zisanu.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chenjerani namondwe akhoza kubuka panyanja yamchere

MBC Online

WFP launches El Nino food insecurity response

McDonald Chiwayula

‘Boma ligwirane manja ndi opanga fetereza wa Mbeya’

Paul Mlowoka
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.