Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

APM wabwera kumudzi

Prezidenti wakale wadziko lino, Professor Peter Mutharika, wabwerera kuno kumudzi lero masanawa.

A Mutharika, omwenso ndi mtsogoleri wachipani chotsutsa cha Democratic Progressive, afika kuno kumudzi kudzera kubwalo landege la Chileka munzinda wa Blantyre.

Poyambirira, akuluakulu a chipanichi adatsutsa zoti a Mutharika ali m’dziko la South Africa pomwe wayilesi ya MBC idafotokoza zakuchoka kwa mtsogoleriyu.

Mmneneri wachipani cha DPP, a Shadreck Namalomba, adakanitsitsa zoti a Mutharika achoka m’dziko muno kufikira pomwe mlembi wamkulu wachipanichi, a Peter Mukhito, anatulutsa kalata yovomereza kuti a Mutharika alidi kunja kwa dziko lino.

Panali mphekesera yoti a Mutharika amalandira thandizo la mankhwala m’dziko la South Africa ngakhale kuti chipanichi chimati apita kukagwira ntchito zina.

A Mutharika, omwe ali ndi zaka 86, akhala m’dziko la South Africa kwa sabata ziwiri.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Legislators to continue lobbying for ADMARC recapitalisation

Simeon Boyce

Mia adzudzula mchitidwe owononga zitukuko za madzi

Emmanuel Chikonso

MAREP 9 yathandiza anthu aku Dedza

Madalitso Mhango
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.