Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

USAID yatsanzika mwapamwamba ku Fisheries

Mawu oti pochoka pamsasa saipitsa ndi amene yagwira bungwe la USAID imene yapereka galimoto zitatu zandalama pafupifupi K380 million ndi katundu wina ku nthambi yoona za nsomba.

Galimotozi zimagwira ntchito mupulojekiti yazaka zisanu yobwezeretsa chilengedwe ndikuwonetsetsa kuti nsomba ya Chambo siikutha munyanja ya Malawi.

Malinga ndi a Daniel Jamu, mkulu wantchitoyi, galimotozi pamodzi ndi katundu wina zithandiza kupitsitsa patsogolo ntchito zanthambi ya Fisheries.

M’modzi mwa akuluakulu ku nthambi ya Fisheries, a Hastings Zidana, ayamikira USAID kudzera mu pulojekiti ya REFRESH kaamba kamphatsozi komanso ntchito yomwe agwira munyanja ya Malawi muzaka zisanuzi.

Kafukufuku waonetsa kuti Chambo chachuluka tsopano munyanja ya Malawi.

 

Related posts

Bungwe lathandiza maanja 20,000 kuthana ndi njala

Alinafe Mlamba

“Ndabwela kudzagwira ntchito” — Uladi Mussa

Mayeso Chikhadzula

Tifalitse uthenga wa matenda a TB ndi Khate — Madam Chakwera

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.