Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Khonsolo ya BT ikumanga zikwangwani m’malire a mnzindawu

Khonsolo ya mnzinda wa Blantyre yakhazikitsa ntchito yomanga zikwangwani zodziwitsa anthu kuti akulowa kapena kutuluka munzindawu.

Pokhazikitsa ntchitoyi kwa Kameza, mfumu ya mnzindawu, a Joseph Makwinja, anati kudziwa malile a mnzinda ndi kofunika kaamba kakuti adindo ndi anthu ena azidziwa kokapereka madandaulo koyenera.

Mu ntchitoyi, zikwangwani zisanu ndi chimodzi ndi zimene akuyembekezera kuzimanga m’mbali zonse za misewu ikuluikulu yolowa ndi kutuluka ku Blantyre monga ku Green Corner pamsewu opita m’boma la Chikwawa.

Ntchitoyi ndi ya ndalama zoposa K5 million ndipo ayigwira ndi thandizo lochokera ku kampani yopanga simenti ya Njereza.

Olemba: Naomi Kamuyango

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MACRA donates 15 computers to Blantyre Teachers’ College

Chisomo Break

‘Horticulture production key to achieving Malawi 2063′

MBC Online

Lack of information on Arbitration Centres is a challenge in Africa — Justice Minister

Austin Fukula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.