Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Khonsolo ya BT ikumanga zikwangwani m’malire a mnzindawu

Khonsolo ya mnzinda wa Blantyre yakhazikitsa ntchito yomanga zikwangwani zodziwitsa anthu kuti akulowa kapena kutuluka munzindawu.

Pokhazikitsa ntchitoyi kwa Kameza, mfumu ya mnzindawu, a Joseph Makwinja, anati kudziwa malile a mnzinda ndi kofunika kaamba kakuti adindo ndi anthu ena azidziwa kokapereka madandaulo koyenera.

Mu ntchitoyi, zikwangwani zisanu ndi chimodzi ndi zimene akuyembekezera kuzimanga m’mbali zonse za misewu ikuluikulu yolowa ndi kutuluka ku Blantyre monga ku Green Corner pamsewu opita m’boma la Chikwawa.

Ntchitoyi ndi ya ndalama zoposa K5 million ndipo ayigwira ndi thandizo lochokera ku kampani yopanga simenti ya Njereza.

Olemba: Naomi Kamuyango

Related posts

DIGC hailed for promoting food sustainability

Rabson Kondowe

Ndende zisintha – Boma

Rabson Kondowe

Malawi’s infrastructural development promising

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.