Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Local Local News Nkhani

Unduna wazantchito watseka mbali ina ya Makandi Tea Estate

Unduna wa zantchito, watseka mbali ina ya Makandi Tea Estate imene ili m’boma la Thyolo chifukwa chophwanya ena mwa malamulo antchito.

Mbaliyi ndi kumene kuli minda ya tiyi ndipo kumadziwika kuti ku 17 A.

Mwazina, a Mumba apeza kuti pamalopa, palibe madzi aukhondo, zimbudzi komanso ogwira ntchito ake alibe zipangizo zowatetezera pamene akugwira ntchito yawo.

Pakadali pano, ndunayi yapereka masiku asanu ndi awiri kuti kampaniyo ikhale itakonza zolakwikazo komanso alamula eni kampaniyo kuti apereke malipiro onse a ogwira ntchito kumbali yomwe ayitsekayi ngakhale kuti sakugwira ntchito.

Mmodzi mwa akuluakulu a kampaniyo, a Joe Palani, ati ayetsetsa kukonza zonse zolakwika mmasikuwo.

A Mumba akuyendera kampani za m’chigawo cha ku m’mwera potsatira madandaulo amene anthu ochuluka kuphatikizapo ogwira ntchito m’malowa akhala akupereka.

 

Related posts

Level 1 Hockey Coaching Course commences in Blantyre

Romeo Umali

Talandira K6 miliyoni koma siyokwanira — Silver Strikers

Romeo Umali

Global austerity crisis strangles public services across Africa

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.