Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Development Local News Nkhani

Tisiya kutaya mkaka, alimi atero

Alimi a ng’ombe za mkaka a ku Mangunda m’boma la Thyolo ati akuyembekeza kuti phindu la ulimi wawo lichuluka kaamba kakuti pa malowa ayikako magetsi a mphamvu ya dzuwa.

Izi zikudza pamene alimiwa alandira thandizo la ndalama zokwana K107 million kuchokera ku TRADE Programme, ndondomeko ya boma yothandiza alimi.

Msungichuma wa gulu la alimiwa, a Elias Piringu, wati magetsi akathima amataya mkaka okwana malita 4000 ndi chifukwa anapempha thandizo la magetsiwa komanso mapampu amadzi.

 

Related posts

Chakwera reaffirms commitment to development

Rabson Kondowe

Analysts hail Chakwera’s cabinet reshuffle

Romeo Umali

Tabitha wakankha chikopa mogometsa mu February ku France

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.