Malawi Broadcasting Corporation
Health Local Local News Nkhani

‘Kukwinimbira ndi vuto lalikulu m’Malawi’

Ana atatu mwa 100 alionse ndi okwinimbira m’dziko muno, kafukufuku amene achita pa sukulu ya ukachenjede ya LUANAR watsimikizira izi.

M’modzi mwa akuluakulu pa sukuluyi, a Alexander Kalimbira, amanena izi mu mzinda wa Lilongwe pa msonkhano wa adindo osiyanasiyana owunikila nkhani zakadyedwe komanso mavuto ake.

Iwo anati zimenezi zikuonetsa kuti dziko la Malawi ati silikuchita bwino pothana ndi vuto la ku kwinimbira.

Komabe a Kalimbira ati ngakhale izi zili chomwechi, dziko lino likuyesetsa kulimbana ndi vutoli kusiyana ndi momwe zinalili kale zomwe akuti ndi chizindikiro kuti kusitha kutha kukhalapo ngati adindo osiyanasiyana atatengapo gawo pothana ndi vutoli.

 

Related posts

Msilikali Sacco AGM approves K156M dividends payout

Yamikani Simtowe

Nsanje Council for adoption of modern farming techniques

Rabson Kondowe

Immigration female staff, spouses cheer special needs children

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.