Malawi Broadcasting Corporation
Health Local Local News Nkhani

‘Kukwinimbira ndi vuto lalikulu m’Malawi’

Ana atatu mwa 100 alionse ndi okwinimbira m’dziko muno, kafukufuku amene achita pa sukulu ya ukachenjede ya LUANAR watsimikizira izi.

M’modzi mwa akuluakulu pa sukuluyi, a Alexander Kalimbira, amanena izi mu mzinda wa Lilongwe pa msonkhano wa adindo osiyanasiyana owunikila nkhani zakadyedwe komanso mavuto ake.

Iwo anati zimenezi zikuonetsa kuti dziko la Malawi ati silikuchita bwino pothana ndi vuto la ku kwinimbira.

Komabe a Kalimbira ati ngakhale izi zili chomwechi, dziko lino likuyesetsa kulimbana ndi vutoli kusiyana ndi momwe zinalili kale zomwe akuti ndi chizindikiro kuti kusitha kutha kukhalapo ngati adindo osiyanasiyana atatengapo gawo pothana ndi vutoli.

 

Related posts

‘Tiganizireni poonjezera ndalama za mtukula pakhomo’

MBC Online

Grain bank initiative can alleviate food insecurity — Nyanya

Romeo Umali

Irrigation farming will end hunger — Chakwera

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.