Malawi Broadcasting Corporation
Health Local Local News Nkhani

‘Kukwinimbira ndi vuto lalikulu m’Malawi’

Ana atatu mwa 100 alionse ndi okwinimbira m’dziko muno, kafukufuku amene achita pa sukulu ya ukachenjede ya LUANAR watsimikizira izi.

M’modzi mwa akuluakulu pa sukuluyi, a Alexander Kalimbira, amanena izi mu mzinda wa Lilongwe pa msonkhano wa adindo osiyanasiyana owunikila nkhani zakadyedwe komanso mavuto ake.

Iwo anati zimenezi zikuonetsa kuti dziko la Malawi ati silikuchita bwino pothana ndi vuto la ku kwinimbira.

Komabe a Kalimbira ati ngakhale izi zili chomwechi, dziko lino likuyesetsa kulimbana ndi vutoli kusiyana ndi momwe zinalili kale zomwe akuti ndi chizindikiro kuti kusitha kutha kukhalapo ngati adindo osiyanasiyana atatengapo gawo pothana ndi vutoli.

 

Related posts

Three bodies recovered in Nsanje canoe accident

Alinafe Mlamba

Trade Ministry to start issuing distributor licences 

Romeo Umali

National Product Magazine urges stronger industry links to boost exports

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.