Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Tisafalitse zopanda umboni

Nduna ya zofalitsa nkhani a Moses Kunkuyu ati nkulakwira malamulo kumafalitsa nkhani zomwe zilibe umboni pankhani ya kusowa kwa ndege yomwe wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Saulos Chilima anakwera.

A Kunkuyu ati nthawi ino, ndi nthawi yoti tigwirane manja ndikupemphera ngati dziko kuti omwe akusaka ndege yi athe kubooleza.

Ndunayi yati bungwe la MACRA lalumikizana ndi mabungwe ena monga la ku Zambia komanso ku Angola kuti athandizire kupeza komwe ndege yi yagwera.

Iwo ati boma molumikizana ndi maiko ena achi ta chilichonse chothekera kusaka komwe ndege yi ili.

 

Related posts

‘Inflation Shows Signs of Stabilisation, But Risks Remain’– Analysts

MBC Online

Tell more stories at local level, DIOs urged

Romeo Umali

Ochita malonda apempha ngongole kwa President Chakwera

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.