Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

Tililire Mulungu — Bishop Nyirenda

Bishop Mthandizi Suzgo Nyirenda wa Diocese ya Mzuzu mu mpingo wa Katolika wapempha aMalawi kuti alilire Mulungu ndi cholinga choti dziko lino lilandire mayankho pa zovuta zosiyanasiyana.

Iwo anatinso kutsogoza pemphero mu zinthu zonse kuphatikizapo kupemphelera atsogoleri ndi za mtengo wapatali.

Bishop Nyirenda amayankhula izi pa mwambo wa misa yomwe imachitikira pa mpingo wa Katolika wa St. Peters mu mzinda wa Mzuzu.

Iwo anati atsogoleri ali ngati chotengera, koma mwini wake opereka zosowa za anthu ndi Mulungu.

Potsindika pa nkhaniyi Bishop Nyirenda analalikira pa mau ochokera m’buku la Eksodo mutu 16 pomwe pali nkhani ya Mose yemwe Mulungu anamugwiritsa ntchito kuti atsogolele ana a Israeli.

Olemba: Jackson Sichali

Related posts

Civil society hails 30 years of gender equality progress in Malawi

Rabson Kondowe

CHAKWERA, MNANGAGWA ATTEND IAFT 2023

MBC Online

Kamtukule alowa chipani cha MCP

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.