Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Takhumudwa posawasankha a Navicha – NGOGCN

Bungwe lolimbikitsa kuti amayi adzikhala m’maudindo akuluakulu la NGO Gender Cordination Network lati ladandaula kuti a Mary Navicha, omwe anali mtsogoleri wa aphungu a chipani cha DPP mnyumba ya malamulo  sanawasankhe kukhala mtsogoleri otsutsa boma m’nyumbayi. 

Wapampando wa bungweli, a Maggie Kathewera Banda, anena izi chipani cha DPP chitalengeza kuti chasankha a George Chaponda kukhala pa udindowu.

A Kathewera Banda ati iwo ndi anzawo akhala akuganiza kuti kaamba koti a Navicha akhala akugwirizira udindo otsogolera DPP mnyumba ya malamulo, komanso ngati njira yolimbikitsira amayi m’maudindo akuluakulu, amayenera kuwasankha kuti apitirize pa udindowu.

Akatswiri enanso a ndale monga a Chimwemwe Tsitsi komanso a Hawkins Munyenyembe, ati nawo amayembekezera kuti chipani cha DPP chisankha a Navicha chifukwa anaonetsa kale machawi popereka maganizo mosawopa ndi mosakondera pomwe amatsogolera aphungu a DPP mnyumba ya malamulo.

 

Olemba: Blessings Cheleuka

Related posts

SIGH OF RELIEF, IMF APPROVES ECF FOR MALAWI

McDonald Chiwayula

WESM calls for participation in the fight against climate change

Rabson Kondowe

Mpinganjira apereka mpamba wa malonda kwa achinyamata 30

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.