Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

‘Siyani kufalitsa nkhani zabodza pa imfa ya Dr Chilima’

Achibale a malemu Dr Saulos Chilima apempha aMalawi kuti asiye kufalitsa nkhani zabodza zokhudza imfa ya m’bale wawo, zimene akuti ndi zowawawitsa mtima komanso zobweretsa mkwiyo pakati pawo.

Nsuweni wa Dr Chilima, a Joshua Valera, amayankhula izi pa Misa yapadera lero pa bwalo la Nsipe Catholic m’boma la Ntcheu ndipo anati ndi koyenera kulemekeza mzimu wa malemu Dr Chilima, amene anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, pokhala olimbika pa ntchito zotukula dziko lino.

M’mawu awo, Inkosi ya Makosi Gomani V, inati anthu m’dziko muno ayenera kukhala a chitsanzo chabwino m’magawo onse a moyo, monga momwe adaliri malemu Dr Chilima.

Pamwambo wa Misawu, akubanja la malemu Chilima apereka Mphatso ya mtanda ku Parish ya Nsipe, kumene Dr Chilima ankakonda kupemphera nthawi iliyonse imene amapezeka m’bomalo.

 

Related posts

Health experts urge caution as push for traditional medicine gains momentum

Rabson Kondowe

Japanese to support construction of Kalumpha Primary School blocks in Dedza

Romeo Umali

ROYAL FAMILY GATHERS AT BALMORAL AMID CONCERNS FOR QUEEN’S HEALTH

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.