Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Sitigawana katundu yemwe talanda kwa anthu ogulitsa malonda — Khonsolo ya Lilongwe

Khonsolo ya mnzinda wa Lilongwe yati sizoona kuti ogwira ntchito ku khonsoloyi amagawana katundu yemwe alanda kwa anthu ogulitsa malonda m’malo osayenera.

Mfumu yamnzinda wa Lilongwe, a Richard Banda, alankhula izi pomwe bungwe la Citizen Alliance linachita msonkhano ndi khonsoloyi okambirana zomwe khonsoloyi ikuchita pamavuto ena amunzindawu, omwe bungweli linanena kuti achitepo kanthu.

Malinga ndi a Banda, katundu yemwe amalanda kwa anthu ogulitsa malonda mmalo osayenera amamusunga ndipo amadzamugulitsa pa okushoni.

Pakadali pano, mtsogoleri wa Citizen Alliance, a Baxton Nkhoma, wati ndiokhutira kuti khonsoloyi ikuyesetsa kuthana ndi ena mwa mavuto omwe anawauza kuti achitepo kanthu.

 

Related posts

Ntchisi youths empowered through tailoring

Rabson Kondowe

Malawi ipindula ndi ntchito yotukula luso lazaumoyo

Romeo Umali

Ochita bwino muligi ya CRNL adzilandira K50,000 sabata iliyonse

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.