Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Promise Kamwendo wapepesa!

Osewera wa Premier Bet Dedza Dynamos, Promise Kamwendo, wapempha amene amamutsatira kuti ayiwale zam’mbuyo pa nkhani imene inawutsa mapiri pachigwa posachedwapa atachita mgwirizano osatsatira malamulo ndi timu ya Mighty Mukuru Wanderers m’malo mwa timu ya FCB Nyasa Big Bullets.

Iye anavomereza kuti anaalakwitsa koma wati zimenezi sizinamusokoneze m’kaganizidwe ndipo wayika chidwi chake chonse kuti alimbikire kumwetsa zigoli ku timu ya Premier Bet Dedza Dynamos ndipo ali kale ndi zigoli zisanu ndi zitatu.

Kamwendo amayankhula izi lachitatu atabwelera ku timu yake yakaleyi kutsatira kulamulidwa ndi bungwe la Football Association of Malawi (FAM) kuti atero.

Mphunzitsi wa Dynamos, a Andrew Bunya, anati ndi okondwera kuti Promise wabwerera chifukwa ndi osewera wawo.

Lachitatu, Kamwendo anali limodzi ndi osewera anzake pamene amachita zokonzekera kuti athambitsane ndi timu ya Creck Sporting Loweruka likudzali.

Related posts

Gulu la amayi amapemphero lithandiza odwala, ana aulumali

Romeo Umali

Manoma eriwa elhopwelhopwe yaakumana ni evithevithe

Romeo Umali

Boma lasintha alembi ena muma unduna

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.