Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Promise Kamwendo wapepesa!

Osewera wa Premier Bet Dedza Dynamos, Promise Kamwendo, wapempha amene amamutsatira kuti ayiwale zam’mbuyo pa nkhani imene inawutsa mapiri pachigwa posachedwapa atachita mgwirizano osatsatira malamulo ndi timu ya Mighty Mukuru Wanderers m’malo mwa timu ya FCB Nyasa Big Bullets.

Iye anavomereza kuti anaalakwitsa koma wati zimenezi sizinamusokoneze m’kaganizidwe ndipo wayika chidwi chake chonse kuti alimbikire kumwetsa zigoli ku timu ya Premier Bet Dedza Dynamos ndipo ali kale ndi zigoli zisanu ndi zitatu.

Kamwendo amayankhula izi lachitatu atabwelera ku timu yake yakaleyi kutsatira kulamulidwa ndi bungwe la Football Association of Malawi (FAM) kuti atero.

Mphunzitsi wa Dynamos, a Andrew Bunya, anati ndi okondwera kuti Promise wabwerera chifukwa ndi osewera wawo.

Lachitatu, Kamwendo anali limodzi ndi osewera anzake pamene amachita zokonzekera kuti athambitsane ndi timu ya Creck Sporting Loweruka likudzali.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Akhale atachoka pasanathe masiku khumi ndi anayi – Unduna waza malonda

Mayeso Chikhadzula

Mlimi watola chikwama

MBC Online

Tipitiriza kuthandiza Malawi – IMF

Justin Mkweu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.