Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Promise Kamwendo wapepesa!

Osewera wa Premier Bet Dedza Dynamos, Promise Kamwendo, wapempha amene amamutsatira kuti ayiwale zam’mbuyo pa nkhani imene inawutsa mapiri pachigwa posachedwapa atachita mgwirizano osatsatira malamulo ndi timu ya Mighty Mukuru Wanderers m’malo mwa timu ya FCB Nyasa Big Bullets.

Iye anavomereza kuti anaalakwitsa koma wati zimenezi sizinamusokoneze m’kaganizidwe ndipo wayika chidwi chake chonse kuti alimbikire kumwetsa zigoli ku timu ya Premier Bet Dedza Dynamos ndipo ali kale ndi zigoli zisanu ndi zitatu.

Kamwendo amayankhula izi lachitatu atabwelera ku timu yake yakaleyi kutsatira kulamulidwa ndi bungwe la Football Association of Malawi (FAM) kuti atero.

Mphunzitsi wa Dynamos, a Andrew Bunya, anati ndi okondwera kuti Promise wabwerera chifukwa ndi osewera wawo.

Lachitatu, Kamwendo anali limodzi ndi osewera anzake pamene amachita zokonzekera kuti athambitsane ndi timu ya Creck Sporting Loweruka likudzali.

Related posts

Athana ndi umphawi pokonza sopo

Romeo Umali

Greenbelt yapereka ntchito yomanga Nthola-Ilola

Romeo Umali

Tilime mbewu zambiri zopilira ku n’gamba — Bushiri

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.