Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Pokhala pabwino ndipofunika msukulu’

Mmodzi kwa akuluakulu oona za maphunziro msukulu za m’madera akumidzi m’boma la Blantyre, a Alfred Mphandamkoko, wati malo ophunzira abwino komanso zipangizo zokwanira ndizofunika pokopa ana kuti adzipita ku sukulu komanso kuchita bwino pa maphunziro awo.

Mphandamkoko amayankhula pa sukulu yakatolika ya Mphati ku Machinjiri m’boma la Blantyre pomwe amalandira madesiki a ndalama zokwana K7 million kuchokera ku bungwe losungitsa ndi kubweleketsa ndalama la Polymed Sacco Limited.

Iwo anati pakadali pano boma lili mkati moonjezera midadada yamakalasi msukulu ndipo Mphati ndi imodzi mwa sukulu zimene zipindule ndi ntchitoyi.

Pamenepa iwo apempha mabungwe enanso akufuna kwabwino kuti athandizenso sukuluyo ndi mipando ina pomwe zipinda zophunzilira zikuchuluka.

Polymed Sacco yapereka madesiki  akuluakulu okwana makumi asanu.

 

Olemba: Naomi Kamuyango

Related posts

Concern over illegal mining in Nkhotakota Game Reserve

Romeo Umali

Castel Malawi raises beer prices

Romeo Umali

Batatawala, Thodi immigration case to continue

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.