Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Okhupha mnzake amugwira

Apolisi ku Soche mu mzinda wa Blantyre amanga Mervin Sulemani wa zaka 27 pomuganizira kuti anapha Rizwani Issa pomukhapa pa 21 mwezi uno ku Chinyonga.

Mneneri wa apolisi ya Soche, Aaron Chilala, wati Sulemani akumuganizira kuti ndi yemwe  sabata yathayi, anapita ndi Issa ku nyumba ina ku Chinyonga chakumasana, kenaka atapeza kuti kulibe anthu, anakhapa ndi chikwanje Issa  mpaka kumwalira, kenaka ndikuthawa pagalimoto.

Iye wati apolisi, apezanso galimoto yomwe akuganiza kuti anaigwiritsa ntchito patsikuli number yake MC 6199.

Chilala wati Sulemani wavomela kuti ndiye anapha Issa atamukakamiza kukwera galimoto yake pa Shoprite kupita ku Chinyonga komwe anamupha kenaka ndikumubera ndalama zokwana K1.5 million, cellphone komanso laptop.

Mervin Sulemani amachokera mmudzi mwa Kaleso kwa TA Mbenje ku Nsanje.

Related posts

Boma la Neno lichita bwino polimbana ndi Edzi

Romeo Umali

ACB ARRESTS 3 MRA OFFICIALS

McDonald Chiwayula

INFRASTRUCTURE DEVELOPMENT CRUCIAL FOR TRADE DEVELOPMENT IN AFRICA – CHAKWERA

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.