Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Oganiziridwa kufalitsa nkhani zabodza akhalabe mchitokosi

Bwalo la milandu la Magistrate munzinda wa Lilongwe lati lipitiriza kumva mulandu wa oganiziridwa kuti amafalitsa nkhani zabodza kudzera pa intaneti a Chiyanjano Mbedza, Lachiwiri pa 30 July 2024.

Bwaloli lati a Chiyanjano Mbedza akhalabe mchitokosi kufikira Lachiwiri nthawi ya 2 koloko masana polola oyimira boma pa milandu kumalizitsa ntchito yofufuza yomwe yangotsala yochepa.

A Mbedza akuwaganizira kuti pa 25 June 2024 anafalitsa uthenga wabodza pa intaneti okhudza imfa ya malemu Dr Saulos Chilima.

Powerenga chikalata cha chigamulochi mmalo mwa oweruza, a Rhodrick Michongwe, a Benaderta Kalua anati izi ndizotsutsana ndi gawo 60 la malamulo aakulu oyendetsera dziko lino.

Olemba ndikujambula: Emmanuel Chikonso ndi Thokozani Jumpha.

Related posts

Ulendo wotsiriza wa Dr Chilima wayambika kupita ku Nsipe

Mayeso Chikhadzula

A Chisale akuyankha mulandu

Romeo Umali

Ogwira ntchito ku Premier Bet wamangidwa atachitila juga ndalama za kampani

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.