Malawi Broadcasting Corporation
Environment Local News Nkhani

Namondwe Chido wakula mphamvu

Nthambi yoona za ngozi zogwa mwadzidzidzi ya DoDMA yati anthu m’dziko muno akhale tcheru komanso atsatire malangizo malinga ndi malipoti okhudza namondwe Chido amene akuyenda m’nyanja ya mchere (Indian Ocean).

Ofalitsa nkhani ku DoDMA, a Chipiliro Khamula, ati nthambi yoona za nyengo yalosera kuti namondweyu wakula mphamvu ndipo akuyembekezeka kuomba pa gombe la Nacala m’dziko la Mozambique Lamulungu likudzali.

Malinga ndi nthambi yoona za nyengoyi, kuwomba kwa namondweyu kutha kudzetsa mvula yochuluka komanso kusefukira kwa madzi m’madera ena a mdziko muno kuyambira Lamulungu kapena Lolemba pa 16 December.

Pa chifukwachi, DoDMA yapemphanso anthu amene amakhala m’malo amene mumasefukira madzi kuti asamukire ku mtunda kuti ateteza miyoyo komanso katundu.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Tigers’ terror: Massacre at Chichiri Stadium

MBC Online

Usi in Tangier Morocco

McDonald Chiwayula

Musangodalira ulimi okha, bungwe la We Effect latero

Aisha Amidu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.