Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Mwana wa Standard 5 wadzipha atamuletsa kuchita zibwenzi

Mtsikana wazaka 15, Eneles Namusanyo, yemwe anali sitandade 5, wadzipha pokwiya chifukwa chodzudzulidwa khalidwe la zibwenzi.

Ofalitsankhani zapolisi ku Mulanje, Innocent Moses, wati mtsikanayo anali pachibwenzi ndi mnyamata wina ndipo mayi ake atadziwa izi, anakhala naye pansi kumulangiza kuti asamachite khalidweli.Kenako mayiwo anachoka pakhomopo ndipo pobwera sanamupeze mwana wawoyo mpaka tsiku lotsatira.

Kutacha, anthu anamupeza atadzimangilira ku denga la nyumba yawo.

Malemuyu anali wa mmudzi wa Ngongondole, mfumu yaikulu Mabuka m’boma la Mulanje.

Related posts

Manoma eriwa elhopwelhopwe yaakumana ni evithevithe

Romeo Umali

Muslims in Mangochi observe Eid with renewed hope amid natural calamities

Romeo Umali

Culture can help achieve Malawi 2063

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.