Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Mwana wa Standard 5 wadzipha atamuletsa kuchita zibwenzi

Mtsikana wazaka 15, Eneles Namusanyo, yemwe anali sitandade 5, wadzipha pokwiya chifukwa chodzudzulidwa khalidwe la zibwenzi.

Ofalitsankhani zapolisi ku Mulanje, Innocent Moses, wati mtsikanayo anali pachibwenzi ndi mnyamata wina ndipo mayi ake atadziwa izi, anakhala naye pansi kumulangiza kuti asamachite khalidweli.Kenako mayiwo anachoka pakhomopo ndipo pobwera sanamupeze mwana wawoyo mpaka tsiku lotsatira.

Kutacha, anthu anamupeza atadzimangilira ku denga la nyumba yawo.

Malemuyu anali wa mmudzi wa Ngongondole, mfumu yaikulu Mabuka m’boma la Mulanje.

Related posts

Immigration officers picked for questioning

Rabson Kondowe

Super League soldiers fall

Romeo Umali

Kaonga to be honoured as Sharda expands scholarships for Malawians

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.