Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Mwana wa Standard 5 wadzipha atamuletsa kuchita zibwenzi

Mtsikana wazaka 15, Eneles Namusanyo, yemwe anali sitandade 5, wadzipha pokwiya chifukwa chodzudzulidwa khalidwe la zibwenzi.

Ofalitsankhani zapolisi ku Mulanje, Innocent Moses, wati mtsikanayo anali pachibwenzi ndi mnyamata wina ndipo mayi ake atadziwa izi, anakhala naye pansi kumulangiza kuti asamachite khalidweli.Kenako mayiwo anachoka pakhomopo ndipo pobwera sanamupeze mwana wawoyo mpaka tsiku lotsatira.

Kutacha, anthu anamupeza atadzimangilira ku denga la nyumba yawo.

Malemuyu anali wa mmudzi wa Ngongondole, mfumu yaikulu Mabuka m’boma la Mulanje.

Related posts

Malawi concludes China – Africa Economic Trade Expo 2024 with strong Trade and Investment gains

Romeo Umali

MCP ikufuna zipani zidzichita misonkhano mwaufulu

Rabson Kondowe

NRB targets over 30,000 registrations in Rumphi

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.