Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Muyembekezere ntchito zachitukuko zochuluka – Mia

Phungu wadera la Chikwawa Nkombezi, a Abida Mia yati aMalawi ayembekezere ntchito zachitukuko zochuluka pansi pa utsogoleri wa Dr. Lazarus Chakwera.

Phunguyi yemwenso ndi nduna yoona zamadzi ndi ukhondo yanena izi pa bwalo lasukulu ya sekondale yoyendera ya Nkumaniza m’bomali pomwe amachititsa msonkhano wachitukuko.

Pankhani ya ku dera lawo, iwo ati apitiriza kukonza misewu, kulimbikitsa ntchito zamaphunziro, zaukhondo komanso zachitetezo mderali.

Mmau ake, bwanankubwa wa boma la Chikwawa, a Nurdin Kamba wayamikira phunguyi  kuti ndi phungu amene amagwiritsa bwino ntchito ndalama za thumba lachitukuko la Constituency Development Fund (CDF).

A  Kamba atinso a Mia amayamba afunsa za zitukuko zomwe anthu ku dera lawo akufuna zomwe ati ndi chitsanzo chabwino pa nkhani yotumikira anthu.

Related posts

Galimoto 40 zonyamula mafuta zafika m’dziko muno, zinanso 70 zifika – NOCMA

Rabson Kondowe

NBS hikes charity shield prize money

Romeo Umali

Mtumbuka pleads with corporate world to support Netball

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.