Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

BJ apereka uthenga wa chiyembekezo ku Chiradzulu

Mkhalakale pa ndale yemwenso ndi m’modzi wa akuluakulu a chipani cholamula cha Malawi Congress (MCP) a Brown Mpinganjira apereka uthenga wachiyembekezo kwa anthu akudera la ku mmawa m’boma la Chiradzulu kudzera ku msonkhano omwe anachititsa mderali.

A Mpinganjira omwenso amadziwika ndi dzina loti BJ achititsa msonkhano pa bwalo la zamasewero la sukulu ya pulaimale ya Bandawe.

Mwa zina a Mpinganjira ati boma likuchita chirichonse chotheka pothana ndi mavuto omwe anthu akukumana nawo.

“Vuto lina lomwe anthuwa akukumana nalo ndi kusowa kwa chakudya,” anatero a Mpinganjira.

Pakadali pano a Mpinganjira ati boma lichita chotheka popereka chakudya komanso ndalama kudzera mu ndondomeko ya Mtukula Pakhomo kuti anthuwa akwanitse kugula zinthu zofunika.

Ena mwa atsogoleri omwe anali nawo pa msonkhanowu ndi wachiwiri kwa mkulu owona za achinyamata mchipani cha MCP a Blessings Chilembwe.

 

Olemba: Timothy Kateta  

Related posts

2023 Castel Cup Awards are on!

Romeo Umali

NCIC conference to tackle quality and construction delays

Rabson Kondowe

Zipani za ndale azipempha kuti ziyanjane pa mwambo oyika maliro

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.