Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MUST ichititsa chionetsero cha chikhalidwe

Sukulu ya ukachenjede ya MUST m’boma la Thyolo yakonzeka kuchititsa chionetsero cha chikhalidwe, kafukufuku ndi luso cha chaka chino, kuchokera pa 4 mpaka pa 5 October. 

Ichi chikhala chionetsero chachiwiri kuchoka pomwe anakhazikitsa zochitikazi chaka chatha.

Malinga ndi mkulu wa zamaphunziro a chikhalidwe ku MUST, Atikonda Mtenje-Mkochi, chiyembekezo chawo ndi chakuti chionetserocho chithandiza kuti luso lomwe likugwirizana ndi chikhalidwe likhale laphindu pa chitukuko cha dziko lino.

Mwazina, pa chionetserocho padzakhala zoimbaimba za akatswiri monga Jetu.

Mutu wa chionetserocho chaka chino ndi Chikhalidwe: Nsanamira ya Chitukuko.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Faith leaders, citizens welcome Dedza Town Council status

Sothini Ndazi

TIMVETSE

McDonald Chiwayula

NEEF yakhazikitsa ngongole ya ulimi wa mthilira

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.