Malawi Broadcasting Corporation
Business Local Local News Nkhani

MBS itsekula sitolo zotsatira malamulo

Ofalitsa nkhani ku bungwe la Malawi Bureau of Standards (MBS), a Wazamazama Katatu, ati bungweli likutsegula sitolo zimene eni ake awaitana kuti akonza mavuto amene analipo.

A Katatu ati sitolozi aziunikanso ngati zakwaniritsa kufikira ndondomeko za ukhondo zimene bungweli limafuna.

Iwo ati sitolo zimene sizikwaniritsa malamulo a ukhondo ndi mfundo za bungweli zikhala chitsekere mpakana pamene atakonze mavutowa.

Mkulu wa sitolo ya Panda ku Area 49 mumzinda wa Lilongwe, a Aaron Mkwezalamba, anati iwo akonza mavuto onse amene analipo m’sitolo yawo monga kupenta komanso kuchotsa mafiliji oonongeka, mwa zina.

A Mkwezalamba ati kuyendera kwa bungwe la MBS mu sitolo yawo kwa waunikira zina zimene samadziwa ndipo ati aonetsetsa kuti akutsata malamulo a ukhondo a bungweli kupita chitsogolo.

Kufikila lero m’mawa, MBS yalandira pempho kuchokera kusitolo zinayi zomwe zinatsekedwa Lolemba kuti akaziyenderenso.

Related posts

Zomba prepared for disasters — DPD

MBC Online

Tidziwapempherera

Romeo Umali

Increase safety net allocations – World Bank

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.