Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Mayi amunjata pofuna kulowetsa chamba kundende

Apolisi munzinda wa Zomba amanga a Jessie Mpanira, 35, powaganizira kuti amafuna kulowetsa chamba ku ndende ya Zomba Maximum.

Wachiwiri kwa ofalitsa nkhani za polisi ya Zomba, a Andrew Mwale, ati mayiyu anapita ku ndendeko kuti akawone mulamu wake amene akugwira ukayidi kwa moyo wake wonse.

Malinga ndi a Mwale, mayiyo anatenga nsima imene anabisamo fodya wamkuluyo.

Monga mwa malamulo, oyang’anira pa ndendepo anayamba kuyiwunika nsimayo asanakayipereke ndipo anazindikira kuti mayi Mpanira anabisa chamba mkati mwa nsimayo.

Amene akuwaganizirawa ndi a m’mudzi wa Duncan, mfumu yayikulu Malemia m’boma la Zomba.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Tilitonse Foundation committed to empowering partners

MBC Online

Tanzania church urges nations to aid communities affected by disasters

Rudovicko Nyirenda

Malawi earmarked for phase 3 of TB vaccine trial

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.