Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Mayi amunjata pofuna kulowetsa chamba kundende

Apolisi munzinda wa Zomba amanga a Jessie Mpanira, 35, powaganizira kuti amafuna kulowetsa chamba ku ndende ya Zomba Maximum.

Wachiwiri kwa ofalitsa nkhani za polisi ya Zomba, a Andrew Mwale, ati mayiyu anapita ku ndendeko kuti akawone mulamu wake amene akugwira ukayidi kwa moyo wake wonse.

Malinga ndi a Mwale, mayiyo anatenga nsima imene anabisamo fodya wamkuluyo.

Monga mwa malamulo, oyang’anira pa ndendepo anayamba kuyiwunika nsimayo asanakayipereke ndipo anazindikira kuti mayi Mpanira anabisa chamba mkati mwa nsimayo.

Amene akuwaganizirawa ndi a m’mudzi wa Duncan, mfumu yayikulu Malemia m’boma la Zomba.

 

Related posts

MBC’s Top of the Class gets K10M boost from MBS

Rabson Kondowe

KATINJI RETURNS TO SILVER STRIKERS

Romeo Umali

CHOLERA OUTBREAK IN MULANJE LINKED TO CROSS-BORDER TRANSMISSION

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.